Loweruka, August 9
Ngati munthu akufuna kunditsatira, adzikane yekha ndipo anyamule mtengo wake wozunzikirapo nʼkupitiriza kunditsatira tsiku ndi tsiku.—Luka 9:23.
N’kutheka kuti inuyo mwakumana ndi mavuto monga kutsutsidwa ndi achibale, kapenanso mwalolera kuti musakhale ndi zinthu zambiri n’cholinga choti muziika zinthu zokhudza Ufumu pamalo oyamba. (Mat. 6:33) Ngati ndi choncho, dziwani kuti Yehova amaona zimene mukuchita pomutumikira mokhulupirika. (Aheb. 6:10) Mwina inunso mwaona kukwaniritsidwa kwa mawu a Yesu akuti: “Palibe amene wasiya nyumba, azichimwene, azichemwali, amayi, abambo, ana kapena minda chifukwa cha ine komanso chifukwa cha uthenga wabwino, amene panopa sadzapeza zochuluka kuwirikiza maulendo 100 mʼnthawi ino. Iye adzapeza nyumba, azichimwene, azichemwali, amayi, ana ndi minda, komanso adzazunzidwa, ndipo mʼnthawi imene ikubwerayo, adzapeza moyo wosatha.” (Maliko 10:29, 30) Madalitso amene mungapeze ndi aakulu kuposa zimene munadzimana.—Sal. 37:4. w24.03 10:5
Lamlungu, August 10
Mnzako weniweni amakusonyeza chikondi nthawi zonse, ndipo ndi m’bale amene anabadwa kuti akuthandize pakagwa mavuto.—Miy. 17:17.
Pa nthawi imene Akhristu a ku Yudeya ankavutika ndi njala yaikulu, Akhristu a mumpingo wa ku Antiokeya wa ku Siriya “anatsimikiza mtima kutumiza thandizo kwa abale a ku Yudeya, aliyense mogwirizana ndi zimene akanakwanitsa.” (Mac. 11:27-30) Ngakhale kuti Akhristu omwe anakhudzidwa ndi njalayi ankakhala kutali, Akhristu a ku Antiokeya anali atatsimikiza mtima kuti awathandize. (1 Yoh. 3:17, 18.) Ifenso masiku ano tingasonyeze chifundo ngati Akhristu anzathu akhudzidwa ndi ngozi zam’chilengedwe kapena mavuto ena aakulu. Tingachitepo kanthu mofulumira, mwina pofunsa akulu ngati tingagwire nawo ntchito yopereka thandizo, popereka ndalama zothandiza pa ntchito yapadziko lonse kapenanso popempherera amene akhudzidwa. Tingafunikenso kuthandiza abale ndi alongo athu kupeza zofunikira pa moyo. Choncho tiyeni tiyesetse kuti pamene Mfumu yathu, Khristu Yesu, adzabwere kudzapereka chiweruzo, adzatipeze tikusonyeza chifundo ndipo adzatiuze kuti ‘tilowe mu Ufumu.’—Mat. 25:34-40. w23.07 29:9-10, 12
Lolemba, August 11
Anthu onse adziwe kuti ndinu ololera.—Afil. 4:5.
Yesu ankatsanzira Yehova pa nkhani yololera. Iye anatumizidwa padziko lapansili kuti akalalikire kwa “nkhosa zotayika za nyumba ya Isiraeli.” Komabe iye anasonyeza kuti ndi wololera pamene ankachita utumiki wake. Pa nthawi ina, mayi wina yemwe sanali wa Chiisiraeli anamupempha kuti achiritse mwana wake wamkazi, yemwe anali atagwidwa ndi ‘chiwanda chimene chinkamuzunza mwankhanza.’ Mwachifundo Yesu anachita zomwe mayiyo anamupempha ndipo anamuchiritsira mwana wakeyo. (Mat. 15:21-28) Taganiziraninso chitsanzo china. Chakumayambiriro kwa utumiki wake, Yesu ananena kuti:“Aliyense amene adzandikane . . . , inenso ndidzamukana.” (Mat. 10:33) Komatu Yesu sanamusiye Petulo ngakhale kuti Petuloyo anali atamukana maulendo angapo. Ankadziwa kuti Petulo anali atalapa komanso anali wokhulupirika. Ataukitsidwa, iye anaonekera kwa Petulo ndipo mwachidziwikire anamutsimikizira kuti anamukhululukira komanso kuti amamukonda. (Luka 24:33, 34) Onse awiri, Yehova Mulungu komanso Yesu Khristu ndi ololera. Nanga bwanji ifeyo? Yehova amayembekezera kuti ifenso tizikhala ololera. w23.07 32:6-7