7 Kenako Mose anaitana Yoswa nʼkumuuza pamaso pa Aisiraeli onse kuti: “Limba mtima ndipo uchite zinthu mwamphamvu,+ chifukwa iwe ndi amene udzalowetse anthu awa mʼdziko limene Yehova analumbira kwa makolo awo kuti adzawapatsa. Ndipo iwe ndi amene udzawagawire dzikolo kuti likhale cholowa chawo.+