-
Salimo 81:11, 12Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
11 Koma anthu anga sanamvere mawu anga,
Isiraeli sanafune kundigonjera.+
-
-
Yeremiya 7:24-26Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
24 Koma iwo sanamvere kapena kutchera khutu.+ Mʼmalomwake, anayenda motsatira zofuna zawo. Mouma khosi anatsatira zofuna za mtima wawo woipawo,+ moti anabwerera mʼmbuyo mʼmalo mopita patsogolo, 25 kuchokera tsiku limene makolo anu anatuluka mʼdziko la Iguputo mpaka pano.+ Choncho ndinapitiriza kukutumizirani atumiki anga onse omwe ndi aneneri, ndinkawatumiza tsiku lililonse, mobwerezabwereza.*+ 26 Koma iwo anakana kundimvera ndipo sanatchere khutu lawo.+ Mʼmalomwake anaumitsa khosi lawo ndipo ankachita zinthu zoipa kuposa makolo awo.
-