-
2 Mbiri 36:15, 16Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
15 Yehova Mulungu wa makolo awo anapitiriza kuwachenjeza kudzera mwa atumiki ake. Ankawachenjeza mobwerezabwereza chifukwa ankamvera chisoni anthu akewo ndiponso malo ake okhala. 16 Koma iwo anapitiriza kunyoza atumiki a Mulungu woona,+ kunyoza mawu ake+ ndiponso kuseka aneneri ake.+ Iwo anafika poti panalibenso chiyembekezo choti angathe kuchiritsidwa. Kenako Yehova anawakwiyira kwambiri nʼkuwalanga.+
-
-
Yesaya 42:24, 25Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
24 Ndi ndani wachititsa kuti Yakobo alandidwe katundu wake
Ndiponso kupereka Isiraeli kwa anthu olanda?
Kodi si Yehova amene iwo amuchimwira?
25 Choncho Mulungu anapitiriza kuwakhuthulira ukali ndi mkwiyo wake,
Anawabweretsera nkhondo yoopsa.+
Moto unapsereza chilichonse chimene anali nacho, koma iwo sanalabadire.+
Motowo unapitiriza kuwawotcha koma iwo sizinawakhudze.+
-