Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • 2 Mbiri 36:15, 16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Yehova Mulungu wa makolo awo anapitiriza kuwachenjeza kudzera mwa atumiki ake. Ankawachenjeza mobwerezabwereza chifukwa ankamvera chisoni anthu akewo ndiponso malo ake okhala. 16 Koma iwo anapitiriza kunyoza atumiki a Mulungu woona,+ kunyoza mawu ake+ ndiponso kuseka aneneri ake.+ Iwo anafika poti panalibenso chiyembekezo choti angathe kuchiritsidwa. Kenako Yehova anawakwiyira kwambiri nʼkuwalanga.+

  • Yesaya 42:24, 25
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Ndi ndani wachititsa kuti Yakobo alandidwe katundu wake

      Ndiponso kupereka Isiraeli kwa anthu olanda?

      Kodi si Yehova amene iwo amuchimwira?

      Iwo anakana kuyenda mʼnjira zake,

      Ndipo sanamvere malamulo* ake.+

      25 Choncho Mulungu anapitiriza kuwakhuthulira ukali ndi mkwiyo wake,

      Anawabweretsera nkhondo yoopsa.+

      Moto unapsereza chilichonse chimene anali nacho, koma iwo sanalabadire.+

      Motowo unapitiriza kuwawotcha koma iwo sizinawakhudze.+

  • Zekariya 1:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Ndakwiyira kwambiri anthu a mitundu ina amene akukhala mosatekeseka.+ Ndawakwiyira chifukwa chakuti ine ndinangokwiyira anthu anga pangʼono,+ koma anthu amenewa anakulitsa kwambiri mavuto a anthu angawo.”’+

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani