-
Deuteronomo 31:16, 17Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
16 Tsopano Yehova anauza Mose kuti: “Iweyo watsala pangʼono kufa,* ndipo anthu awa adzakhala osakhulupirika kwa ine ndipo adzayamba kulambira milungu yachilendo imene ili mʼdziko limene akupita.+ Iwo adzandisiya+ nʼkuphwanya pangano limene ndinapangana nawo.+ 17 Pa nthawi imeneyo mkwiyo wanga udzawayakira+ ndipo ndidzawasiya+ nʼkuwabisira nkhope yanga+ mpaka atawonongedwa.+ Ndiyeno akadzakumana ndi masoka komanso mavuto ambiri adzanena kuti, ‘Masoka amenewatu akutigwera chifukwa chakuti Mulungu wathu sali pakati pathu.’+
-
-
2 Mbiri 36:15, 16Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
15 Yehova Mulungu wa makolo awo anapitiriza kuwachenjeza kudzera mwa atumiki ake. Ankawachenjeza mobwerezabwereza chifukwa ankamvera chisoni anthu akewo ndiponso malo ake okhala. 16 Koma iwo anapitiriza kunyoza atumiki a Mulungu woona,+ kunyoza mawu ake+ ndiponso kuseka aneneri ake.+ Iwo anafika poti panalibenso chiyembekezo choti angathe kuchiritsidwa. Kenako Yehova anawakwiyira kwambiri nʼkuwalanga.+
-