Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • Yeremiya 4:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Mayo ine,* mayo ine!

      Ndikumva kupweteka kwambiri mumtima mwanga.

      Mtima wanga ukugunda kwambiri.

      Sindingathe kukhala chete,

      Chifukwa ndamva kulira kwa lipenga la nyanga ya nkhosa,

      Chizindikiro chochenjeza cha nkhondo.*+

  • Yeremiya 8:18, 19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Chisoni changa nʼchosachiritsika.

      Mtima wanga ukudwala.

      19 Pakumveka mawu olirira thandizo kuchokera kudziko lakutali,

      Kuchokera kwa mwana wamkazi wa anthu anga.

      Iye akuti: “Kodi Yehova sali mu Ziyoni?

      Kapena kodi mfumu yake mulibe mmenemo?”

      “Nʼchifukwa chiyani andikhumudwitsa ndi mafano awo ogoba,

      Ndiponso milungu yawo yachilendo yopanda pake?”

  • Yeremiya 9:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Ndikanakonda mʼmutu mwanga mukanakhala madzi ambiri,

      Ndiponso maso anga akanakhala kasupe wa misozi.+

      Zikanatero, ndikanalira masana ndi usiku

      Chifukwa cha anthu a mtundu wanga amene aphedwa.

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani