Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • Yesaya 1:23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Akalonga ako ndi osamva ndipo amagwirizana ndi anthu akuba.+

      Aliyense wa iwo amakonda ziphuphu ndipo amalakalaka kupatsidwa mphatso.+

      Mwana wamasiye samuweruza mwachilungamo,

      Ndipo ngakhale mlandu wa mkazi wamasiye safuna kuuweruza.+

  • Yeremiya 5:26-28
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 26 Chifukwa pakati pa anthu anga pali anthu oipa.

      Iwo amabisala nʼkumayangʼanitsitsa ngati mmene amachitira wosaka mbalame.

      Amatchera msampha wakupha

      Ndipo amagwira anthu.

      27 Mofanana ndi chikwere chimene chadzaza mbalame,

      Nyumba zawo zadzaza chinyengo.+

      Nʼchifukwa chake iwo ali amphamvu komanso alemera kwambiri.

      28 Iwo anenepa ndipo asalala.

      Akuchita zinthu zoipa zambiri.

      Iwo saweruza mlandu wa ana amasiye mwachilungamo,+

      Pofuna kupeza phindu.

      Ndipo sachitira chilungamo anthu osauka.’”+

  • Mika 2:1, 2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 “Tsoka kwa anthu amene amakonza chiwembu,

      Amene akagona pabedi pawo, amaganizira kuti achite zoipa.

      Ndipo mʼmawa kukacha, amazichitadi.

      Chifukwa ali ndi mphamvu zochitira zimenezo.+

       2 Iwo amalakalaka minda ya anthu ena ndipo amaitenga.+

      Amalakalakanso nyumba za anthu ena nʼkuzitenga.

      Amatenga mwachinyengo nyumba ya munthu,+

      Ndipo amatenganso cholowa cha munthu.

  • Mika 6:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Kodi mʼnyumba ya munthu woipa mukupezekabe chuma chopezedwa mopanda chilungamo?

      Ndiponso muyezo woperewera wa efa* umene ndi wonyansa?

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani