Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • Deuteronomo 28:52
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 52 Adzakuzungulirani nʼkukutsekerani mʼmizinda yanu* mʼdziko lanu lonse, mpaka mipanda yanu yaitali ndi yolimba kwambiri imene mukuidalira itagwa. Adzakuzungulirani ndithu mʼmizinda yanu yonse mʼdziko lanu limene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.+

  • 2 Mafumu 25:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 25 Mʼchaka cha 9 cha ufumu wa Zedekiya, mʼmwezi wa 10, pa tsiku la 10 la mweziwo, Nebukadinezara+ mfumu ya Babulo anabwera ku Yerusalemu pamodzi ndi asilikali ake onse.+ Anabwera kudzamenyana ndi anthu amumzindawo ndipo anamanga msasa komanso mpanda kuzungulira mzinda wonsewo.+

  • Yeremiya 33:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 “Yehova Mulungu wa Isiraeli wanena mawu okhudza nyumba zamumzinda uwu ndiponso okhudza nyumba za mafumu a Yuda, zimene zagwetsedwa chifukwa cha malo okwera omenyerapo nkhondo ndiponso lupanga la adani.+

  • Ezekieli 4:1, 2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 “Iwe mwana wa munthu, tenga njerwa ndipo uiike patsogolo pako. Panjerwapo ujambulepo mzinda wa Yerusalemu. 2 Umenye nkhondo ndi mzindawo+ ndipo umange mpanda womenyerapo nkhondo kuzungulira mzinda wonsewo.+ Umangenso malo okwera omenyerapo nkhondo+ komanso misasa ya asilikali. Uikenso zida zankhondo zogumulira mpanda wa mzindawo kuzungulira mzinda wonsewo.+

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani