Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • 2 Mbiri 36:15, 16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Yehova Mulungu wa makolo awo anapitiriza kuwachenjeza kudzera mwa atumiki ake. Ankawachenjeza mobwerezabwereza chifukwa ankamvera chisoni anthu akewo ndiponso malo ake okhala. 16 Koma iwo anapitiriza kunyoza atumiki a Mulungu woona,+ kunyoza mawu ake+ ndiponso kuseka aneneri ake.+ Iwo anafika poti panalibenso chiyembekezo choti angathe kuchiritsidwa. Kenako Yehova anawakwiyira kwambiri nʼkuwalanga.+

  • Yesaya 65:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  2 Ndatambasula manja anga tsiku lonse kwa anthu amakani,+

      Kwa anthu amene akuyenda mʼnjira yoipa,+

      Potsatira maganizo awo,+

  • Yeremiya 7:24-26
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Koma iwo sanamvere kapena kutchera khutu.+ Mʼmalomwake, anayenda motsatira zofuna zawo. Mouma khosi anatsatira zofuna za mtima wawo woipawo,+ moti anabwerera mʼmbuyo mʼmalo mopita patsogolo, 25 kuchokera tsiku limene makolo anu anatuluka mʼdziko la Iguputo mpaka pano.+ Choncho ndinapitiriza kukutumizirani atumiki anga onse omwe ndi aneneri, ndinkawatumiza tsiku lililonse, mobwerezabwereza.*+ 26 Koma iwo anakana kundimvera ndipo sanatchere khutu lawo.+ Mʼmalomwake anaumitsa khosi lawo ndipo ankachita zinthu zoipa kuposa makolo awo.

  • Yeremiya 35:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Ndinkakutumizirani mobwerezabwereza*+ atumiki anga onse omwe anali aneneri. Ndinkawauza uthenga wakuti, ‘Chonde bwererani ndipo aliyense asiye njira zake zoipa.+ Muzichita zinthu zabwino. Musatsatire milungu ina nʼkumaitumikira. Mukatero mudzapitiriza kukhala mʼdziko limene ndinapatsa inuyo ndi makolo anu.’+ Koma inu simunatchere khutu kapena kundimvera.

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani