-
Yeremiya 25:15Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
15 Yehova Mulungu wa Isiraeli anandiuza kuti: “Tenga kapu iyi ya vinyo wa mkwiyo imene ili mʼdzanja langa ndipo ukamwetse mitundu yonse imene ndikukutumizako.
-
-
Yeremiya 25:19Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
19 Kenako ndinamwetsanso Farao mfumu ya Iguputo, atumiki ake, akalonga ake ndi anthu ake onse+
-
-
Ezekieli 29:2Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
2 “Iwe mwana wa munthu, yangʼana kwa Farao mfumu ya Iguputo ndipo ulosere zoipa zimene zidzachitikire iyeyo ndi dziko lonse la Iguputo.+
-
-
Ezekieli 32:2Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
2 “Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yoimba polira yokhudza Farao, mfumu ya Iguputo ndipo umuuze kuti,
‘Iwe unali ngati mkango waungʼono wamphamvu* wa mitundu ina ya anthu,
Koma wakhalitsidwa chete.
Unali ngati chilombo chamʼnyanja+ chimene chimavundula madzi mwamphamvu mʼmitsinje yako
Nʼkumadetsa madzi ndi mapazi ako ndiponso kuipitsa mitsinjeyo.’
-