-
Ezekieli 23:22, 23Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
22 Choncho iwe Oholiba, Yehova Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: ‘Ndichititsa kuti amuna omwe unkawakonda,+ amene unawasiya chifukwa chonyansidwa nawo akuukire. Ndidzawabweretsa kuchokera kumbali zonse kuti adzakuukire.+ 23 Ndidzabweretsa amuna a ku Babulo,+ Akasidi onse,+ amuna a ku Pekodi,+ a ku Sowa, a ku Kowa pamodzi ndi amuna onse amʼdziko la Asuri. Onsewa ndi anyamata osiririka, abwanamkubwa, achiwiri kwa olamulira, asilikali komanso amuna osankhidwa mwapadera.* Onsewa ndi akatswiri okwera mahatchi.
-