Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • Machitidwe 24
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Machitidwe

      • Milandu imene Paulo ankaimbidwa (1-9)

      • Paulo anadziteteza pamaso pa Felike (10-21)

      • Mlandu wa Paulo unaimitsidwa kwa zaka ziwiri (22-27)

Machitidwe 24:1

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “loya wina.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 23:2
  • +Mac 23:26

Machitidwe 24:5

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mt 5:11; Mac 16:20, 21; 17:6, 7
  • +Lu 23:1, 2
  • +Mt 2:23; Mac 28:22

Machitidwe 24:6

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 21:27, 28

Machitidwe 24:7

Mawu a M'munsi

  • *

    Onani Zakumapeto A3.

Machitidwe 24:10

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Afi 1:7

Machitidwe 24:11

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 21:17, 26

Machitidwe 24:14

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 3:15; Mac 3:13; 2Ti 1:3
  • +Mac 28:23; Aro 3:21

Machitidwe 24:15

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yes 26:19; Mt 22:31, 32; Lu 14:13, 14; Yoh 5:28, 29; 11:25; Ahe 11:35; Chv 20:12
  • +Lu 23:43

Machitidwe 24:16

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 23:1; 1Ak 4:4; Ahe 13:18

Machitidwe 24:17

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +2Ak 8:4

Machitidwe 24:18

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 21:24, 26

Machitidwe 24:19

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 25:16

Machitidwe 24:21

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 23:6

Machitidwe 24:22

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 9:1, 2; 19:9

Machitidwe 24:24

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mt 10:18

Machitidwe 24:25

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 17:30, 31; 2Ak 5:10

Machitidwe 24:27

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 25:9

Malemba Ena

Mac. 24:1Mac 23:2
Mac. 24:1Mac 23:26
Mac. 24:5Mt 5:11; Mac 16:20, 21; 17:6, 7
Mac. 24:5Lu 23:1, 2
Mac. 24:5Mt 2:23; Mac 28:22
Mac. 24:6Mac 21:27, 28
Mac. 24:10Afi 1:7
Mac. 24:11Mac 21:17, 26
Mac. 24:14Eks 3:15; Mac 3:13; 2Ti 1:3
Mac. 24:14Mac 28:23; Aro 3:21
Mac. 24:15Yes 26:19; Mt 22:31, 32; Lu 14:13, 14; Yoh 5:28, 29; 11:25; Ahe 11:35; Chv 20:12
Mac. 24:15Lu 23:43
Mac. 24:16Mac 23:1; 1Ak 4:4; Ahe 13:18
Mac. 24:172Ak 8:4
Mac. 24:18Mac 21:24, 26
Mac. 24:19Mac 25:16
Mac. 24:21Mac 23:6
Mac. 24:22Mac 9:1, 2; 19:9
Mac. 24:24Mt 10:18
Mac. 24:25Mac 17:30, 31; 2Ak 5:10
Mac. 24:27Mac 25:9
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
  • 27
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Machitidwe 24:1-27

Machitidwe a Atumwi

24 Patatha masiku 5, kunafika mkulu wa ansembe Hananiya+ pamodzi ndi akulu ena, komanso munthu wina wodziwa kulankhula,* dzina lake Teritulo. Iwo anayamba kufotokoza mlandu wa Paulo kwa bwanamkubwa.+ 2 Teritulo atapatsidwa mwayi kuti alankhule, anayamba kumuneneza Paulo kuti:

“Tili pa mtendere wambiri chifukwa cha inu, komanso zinthu zikusintha mu mtundu wathuwu chifukwa cha nzeru zanu zoona patali. 3 Choncho nthawi zonse komanso kulikonse, inu Wolemekezeka a Felike, ife timaona nzeru zanuzo ndipo timayamikira kwambiri. 4 Koma kuti ndisakutayitseni nthawi, ndikupempha kuti mutikomere mtima ndipo mumve mawu athu pangʼono. 5 Ife tapeza kuti munthu uyu ndi wovutitsa kwabasi,+ ndipo akuyambitsa zoukira boma+ pakati pa Ayuda padziko lonse. Ndiponso ndi mtsogoleri wa gulu lampatuko la anthu a ku Nazareti.+ 6 Komanso iyeyu ankafuna kudetsa kachisi ndipo tinamugwira.+ 7*⁠—— 8 Mutamufunsa, mungathe kutsimikizira nokha zonse zimene tikunenazi.”

9 Atanena zimenezi Ayuda nawonso analowerera ndipo ankanena motsimikiza kuti zimenezo nʼzoona. 10 Bwanamkubwayo atagwedezera Paulo mutu kuti alankhule, Paulo anayankha kuti:

“Ndikudziwa kuti mwakhala woweruza wa mtundu uwu kwa zaka zambiri. Choncho ndine wosangalala kulankhula podziteteza pa zimene akundinenerazi.+ 11 Inu mukhoza kupeza umboni wakuti masiku 12 sanadutse kuchokera pamene ine ndinapita ku Yerusalemu+ kukalambira Mulungu. 12 Ndipo iwowa sanandipezepo mʼkachisi ndikutsutsana ndi aliyense. Sanandipezenso ndikuyambitsa chipolowe mʼmasunagoge kapena pena paliponse mumzindawu. 13 Ndipo panopa sangathe kukupatsani umboni wa zimene akundinenerazi. 14 Koma chomwe ndikuvomereza kwa inu ndi chakuti: Njira yolambirira imene iwo akuitchula kuti ‘gulu lampatuko,’ ndi imene ine ndikuitsatira potumikira Mulungu wa makolo anga.+ Chifukwa ndimakhulupirira zonse zimene zili mʼChilamulo ndi zimene aneneri analemba.+ 15 Ndipo ine ndili ndi chiyembekezo ngati chimenenso anthu awa ali nacho, kuti Mulungu adzaukitsa+ olungama ndi osalungama omwe.+ 16 Chifukwa cha zimenezi, ndikuyesetsa mwakhama kuti ndikhale ndi chikumbumtima chabwino kwa Mulungu ndiponso kwa anthu.+ 17 Ndiyeno pambuyo pa zaka zambiri, ndinabwera kudzapereka mphatso zachifundo+ kwa anthu a mtundu wanga ndiponso kudzapereka nsembe. 18 Pamene ndinkachita zimenezi, anandipeza mʼkachisi nditadziyeretsa motsatira mwambo.+ Panalibe gulu la anthu kapena phokoso, koma panali Ayuda ena ochokera mʼchigawo cha Asia. 19 Amenewo, akanakhala ndi chifukwa, ndi amene anayenera kubwera kwa inu kudzandiimba mlandu.+ 20 Kapena muwalole anthu ali panowa, afotokoze okha ngati anandipeza ndi mlandu uliwonse pamene ndinaima pamaso pa Khoti Lalikulu la Ayuda. 21 Mawu amodzi okha amene ine ndinanena, pamene ndinaima pakati pawo ndi akuti, ‘Ine lero ndikuweruzidwa chifukwa cha chiyembekezo chakuti akufa adzauka!’”+

22 Popeza Felike ankadziwa bwino nkhani yokhudza Njira imeneyi,+ anaimitsa mlanduwo nʼkunena kuti: “Ndidzagamula mlandu wanuwu akadzafika Lusiya mkulu wa asilikali.” 23 Iye analamula mtsogoleri wa asilikali kuti amusunge mʼndende, koma amupatseko ufulu ndipo azilola anthu a mtundu wake kudzamuthandiza.

24 Patapita masiku angapo, Felike anafika pamodzi ndi mkazi wake Durusila, amene anali Myuda. Ndiyeno Felike anaitanitsa Paulo nʼkumamvetsera pamene ankafotokoza za kukhulupirira Khristu Yesu.+ 25 Koma pamene ankafotokoza zokhudza chilungamo, kudziletsa ndiponso chiweruzo chimene chikubwera,+ Felike anachita mantha ndipo anati: “Basi pita kaye, ndikadzapeza nthawi ndidzakuitananso.” 26 Komanso ankaganiza kuti Paulo amupatsa ndalama. Choncho ankamuitanitsa pafupipafupi nʼkumakambirana naye. 27 Patatha zaka ziwiri, Felike analowedwa mʼmalo ndi Porikiyo Fesito. Koma popeza Felike ankafuna kuti Ayuda azimukonda,+ anangomusiya Paulo mʼndende.

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani