Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • w24.01 103
  • Mfundo Zothandiza Pophunzira

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mfundo Zothandiza Pophunzira
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2024
  • Nkhani Yofanana
  • Tingatani Kuti Mulungu Azisangalala Ndi Kulambira Kwathu?
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • Tizitamanda Yehova Mumpingo
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2019
  • Kuwonjezera Luso Lathu mu Utumiki​—Muzithandiza Ophunzira Anu Kuti Azikonzekera
    Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2018
  • Mungatani Kuti Banja Lanu Likhale Losangalala?​—Mbali Yachiwiri
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2024
w24.01 103

MFUNDO ZOTHANDIZA POPHUNZIRA

Zimene Mungachite Pophunzira Panokha Komanso pa Kulambira kwa Pabanja

Sikuti timangolambira Yehova tikakhala pagulu lalikulu ngati pamisonkhano yampingo, yadera kapena yachigawo koma timamulambiranso monga banja komanso patokha. Izi ndi zina zomwe mungachite mukamaphunzira panokha kapena pa kulambira kwa pabanja:

  • Kukonzekera misonkhano yampingo. Mungaphatikizepo kuphunzira nyimbo komanso kuthandiza onse a m’banja lanu kuti akayankhe.

  • Kuwerenga nkhani ya m’Baibulo. Pambuyo pake mungajambule chithunzi cha nkhani yomwe mwawerengayo kapena kulemba zimene mwaphunzirapo.

  • Kuwerenga pemphero linalake lopezeka m’Baibulo kenako kukambirana mmene lingakuthandizireni kuti mapemphero anu azikhala abwino.

  • Kuonera imodzi mwa mavidiyo athu kenako kukambirana kapena kulemba zimene mwaphunzirapo.

  • Kukonzekera ulaliki, mwinanso kuyeserera zimene mungakachite.

  • Kufufuza zokhudza chilengedwe komanso kuganizira kapena kukambirana zimene mukuphunzirapo zokhudza Yehova.a

a Onani nkhani yakuti “Muziphunzira Zambiri Zokhudza Yehova Poona Chilengedwe Chake” mu Nsanja ya Olonda ya March 2023.

    Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
    • tumizirani
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • zachinsinsi
    • JW.ORG
    • Lowani
    tumizirani