Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • hf section 4
  • Muzigwiritsa Ntchito Bwino Ndalama

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Muzigwiritsa Ntchito Bwino Ndalama
  • Banja Lanu Likhoza Kukhala Losangalala
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • 1 MUZIKHALA NDI BAJETI
  • 2 MUZIKAMBIRANA MOMASUKA
  • Kodi Ndalama ndi Zimene Zimabweretsa Mavuto Onse?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
Banja Lanu Likhoza Kukhala Losangalala
hf section 4
Mwamuna ndi mkazi akukambirana zimene angachite kuti agwiritse ntchito ndalama mwanzeru

MUTU 4

Muzigwiritsa Ntchito Bwino Ndalama

“Zolinga zimakhazikika anthu akakambirana.”—Miyambo 20:18

Tonsefe timafuna ndalama zogulira zinthu zofunika m’banja lathu. (Miyambo 30:8) Paja “ndalama zimatetezera.” (Mlaliki 7:12) Mabanja ambiri amavutika kuti akambirane nkhani za ndalama. Koma musalole kuti ndalama zisokoneze banja lanu. (Aefeso 4:32) Mwamuna ndi mkazi ayenera kukhulupirirana ndiponso kukambirana mmene angagwiritsire ntchito ndalama zawo.

1 MUZIKHALA NDI BAJETI

ZIMENE BAIBULO LIMANENA: “Ndani wa inu amene akafuna kumanga nsanja sayamba wakhala pansi ndi kuwerengera ndalama zimene adzawononge, kuti aone ngati ali ndi ndalama zokwanira kumalizira nsanjayo?” (Luka 14:28) N’zofunika kwambiri kuti muzigwirizana mmene mudzagwiritsira ntchito ndalama zanu. (Amosi 3:3) Muyenera kusankha zinthu zofunika kugula komanso kuchuluka kwa ndalama zimene mungawononge. (Miyambo 31:16) Komanso ngati muli ndi ndalama zokwanira kuti mugule chinachake sikuti muyenera kuchigula basi. Yesetsani kupewa ngongole. Muzingogwiritsa ntchito ndalama zimene muli nazo.—Miyambo 21:5; 22:7.

ZIMENE MUNGACHITE:

  • Mukatsala ndi ndalama pa mapeto pa mwezi, muzikambirana zimene mungachite nazo

  • Ngati ndalama zanu zimakhala zoperewera, kambiranani zimene mungachite kuti musamawononge zambiri. Mwachitsanzo, m’malo mophika chakudya chambiri n’kutaya chotsala, muzingophika chokwanira bwinobwino banja lanulo

Mwamuna ndi mkazi wake akukambirana za zinthu zimene zimawathera ndalama kwambiri

2 MUZIKAMBIRANA MOMASUKA

ZIMENE BAIBULO LIMANENA: “Timasamalira zinthu zonse moona mtima, osati pamaso pa Yehova pokha ayi, komanso pamaso pa anthu.” (2 Akorinto 8:21) Muziuza mwamuna kapena mkazi wanu ndalama zonse zimene mumalandira komanso mmene mumazigwiritsira ntchito.

Muzikambirana kaye musanagwiritse ntchito ndalama zambiri. (Miyambo 13:10) Kukambirana bwinobwino nkhani za ndalama kungathandize kuti muzikhala mwamtendere. Muzionanso kuti ndalama zimene mumapeza ndi za banja lonse osati zanokha.—1 Timoteyo 5:8.

Mwamuna ndi mkazi wake akuona zimene alemba kuti agule

ZIMENE MUNGACHITE:

  • Muzikambirana n’kuona kuchuluka kwa ndalama zimene aliyense angagwiritse ntchito popanda kuuza mnzake

  • Musamadikire kuti pakhale vuto kaye kuti mukambirane za ndalama

MUZIONA NDALAMA MOYENERA

Ndalama n’zofunika koma musalole kuti ziyambitse mavuto m’banja lanu. (Mateyu 6:25-34) Ndalama zambiri si zimene zingachititse kuti mukhale osangalala. Paja Baibulo limati: “Chenjerani ndi kusirira kwa nsanje kwamtundu uliwonse.” (Luka 12:15) Banja lanu ndi lamtengo wapatali kwambiri kuposa chilichonse chimene mungagule ndi ndalama. Choncho muzikhutira ndi zimene muli nazo ndipo muziyesetsa kulimbitsa ubwenzi wanu ndi Mulungu. Mukatero, banja lanu lidzakhala losangalala ndipo mudzasangalatsanso Yehova.—Aheberi 13:5.

DZIFUNSENI KUTI . . .

  • Kodi tingapewe bwanji kukhala ndi ngongole?

  • Kodi ine ndi mwamuna kapena mkazi wanga tinakambirana liti momasuka za ndalama zathu?

    Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
    • tumizirani
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • zachinsinsi
    • JW.ORG
    • Lowani
    tumizirani