Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • lfb sect. 2
  • Mawu Oyamba Gawo 2

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mawu Oyamba Gawo 2
  • Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Chigumula Chisanachitike, Kodi Ndani Anamvera Mulungu Ndipo Ndani Amene Sanamumvere?
    Mverani Mulungu Kuti Mudzapeze Moyo Wosatha
  • Anakwiya Mpaka Anapha M’bale Wake
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • “Anayenda Ndi Mulungu Woona”
    Tsanzirani Chikhulupiriro Chawo
  • “Ngakhale kuti Anafa, Iye Akulankhulabe”
    Tsanzirani Chikhulupiriro Chawo
Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
lfb sect. 2
Nowa akulowetsa zinyama m’chingalawa

Mawu Oyamba Gawo 2

N’chifukwa chiyani Yehova anabweretsa chigumula chimene chinawononga zamoyo zonse? Kale kwambiri anthu asanachuluke padzikoli, Satana anachititsa kuti anthu asamamvere Yehova. Anthu ena monga Adamu, Hava ndi mwana wawo Kaini anasankha kuchita zofuna za Satana. Koma panalinso anthu ena ochepa monga Abele ndi Nowa omwe anasankha kuchita zimene Yehova amafuna. Pofika nthawi ya Nowa anthu ambiri ankachita zoipa, n’chifukwa chake Yehova anawononga dziko loipalo. Chigawochi chitithandiza kudziwa kuti Yehova amaona ngati tasankha kukhala kumbali yake kapena kukhala kumbali ya Satana, ndipo sadzalola kuti Satana alepheretse zolinga zake.

ZIMENE TIPHUNZIRE M’CHIGAWOCHI

  • Tiyenera kukhala anthu amtendere osati achiwawa ngati Satana ndi otsatira ake

  • Tikamamvera Mulungu ngati mmene Nowa anachitira, tidzakhala osangalala komanso tidzapeza moyo wosatha

  • Yehova amaona zonse zimene anthu akuchita. Ndipo amasangalala ndi anthu amene amachita zabwino koma amakwiya ndi anthu ochita zoipa

    Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
    • tumizirani
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • zachinsinsi
    • JW.ORG
    • Lowani
    tumizirani