Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • lfb sect. 7
  • Mawu Oyamba Gawo 7

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mawu Oyamba Gawo 7
  • Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Davide ndi Sauli
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Zimene Zili Mʼbuku la 1 Samueli
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Aisiraeli Anapempha Kuti Akhale ndi Mfumu
    Kodi Baibulo Lili Ndi Uthenga Wotani?
Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
lfb sect. 7
Davide akulanditsa nkhosa kuti zisaphedwe ndi chimbalangondo

Mawu Oyamba Gawo 7

Chigawochi chikufotokoza mbiri ya moyo wa Mfumu Sauli komanso Mfumu Davide. Nkhaniyi inachitika pafupifupi kwa zaka 80. Poyamba Sauli anali wodzichepetsa komanso ankamvera Mulungu. Koma kenako anasintha n’kusiya kutsatira malangizo a Yehova. Zitatero Yehova anamukana ndipo patapita nthawi anauza Samueli kuti adzoze Davide kuti akhale mfumu ya Aisiraeli. Sauli ankachitira nsanje Davide ndipo mobwerezabwereza anayesa kuti amuphe koma Davideyo sanabwezere. Mwana wa Sauli dzina lake Yonatani, ankadziwa kuti Davide wasankhidwa ndi Yehova choncho anakhala wokhulupirika kwa Davideyo. Davide anachita machimo ena akuluakulu koma nthawi zonse ankamvera Yehova akamudzudzula. Ngati ndinu kholo, thandizani mwana wanu kuti aziona kufunika kotsatira malangizo a Mulungu nthawi zonse.

ZIMENE TIPHUNZIRE M’CHIGAWOCHI

  • Yehova amafuna kuti tizimumvera chifukwa chomukonda

  • Sitiyenera kubwezera koma tizidikira kuti Yehova akonze zinthu

  • Tikachita tchimo lalikulu, sitiyenera kubisa

    Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
    • tumizirani
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • zachinsinsi
    • JW.ORG
    • Lowani
    tumizirani