Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • mwb23.07 15
  • Amachita Khama Kuti Atitumikire

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Amachita Khama Kuti Atitumikire
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
  • Nkhani Yofanana
  • Muziyamikira Amuna Amene Yehova Watipatsa Mumpingo
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2024
  • ‘Paulo Anayamika Mulungu, Ndipo Analimba Mtima’
    Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2019
  • Zosankha Zomwe Zimasonyeza Kuti Timadalira Yehova
    Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
  • Kupatsa Kumatichititsa Kukhala Osangalala
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2024
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
mwb23.07 15
Zithunzi zosonyeza woyang’anira dera pa nthawi imene akuchezera mpingo: 1. Akuchititsa msonkhano wokonzekera utumiki. 2. Ali pa msonkhano ndi bungwe la akulu. 3. Ali ndi m’bale wachinyamata mu utumiki.

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Amachita Khama Kuti Atitumikire

Oyang’anira madera ndi akazi awo amasonyeza chikondi chololera kuvutikira anthu amene amawatumikira. Mofanana ndi ena tonse, nawonso amafunikira zinthu zina, nthawi zina amatopa, amafooka komanso amakhala ndi nkhawa. (Yak 5:17) Komabe, mlungu uliwonse iwo amaganizira mmene angalimbikitsire abale ndi alongo a mumpingo umene akuchezera. Kunena zoona, oyang’anira dera amafunika “apatsidwe ulemu waukulu.”​—1Ti 5:17.

Pamene mtumwi Paulo ankakonzekera kupita ku Roma kuti ‘akagawire abale a mpingo wa kumeneko mphatso inayake yauzimu,’ ankayembekezera mwachidwi kuti akalimbikitsane nawo mwa ‘chikhulupiriro chake ndi chawo.’ (Aro 1:11, 12) Kodi munaganizirapo za mmene mungalimbikitsire woyang’anira dera ndi mkazi wake, ngati ali wokwatira?

ONERANI VIDIYO YAKUTI MOYO WA WOYANG’ANIRA DERA AMENE AMATUMIKIRA MADERA A KU MIDZI, KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Kodi oyang’anira madera ndi akazi awo amasonyeza chikondi chololera kuvutikira ena m’njira ziti?

  • Kodi zomwe amachita zakuthandizani bwanji?

  • Kodi tingawalimbikitse bwanji?

    Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
    • tumizirani
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • zachinsinsi
    • JW.ORG
    • Lowani
    tumizirani