Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • w24.06 103
  • Kodi Muli ndi Chikhulupiriro?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Muli ndi Chikhulupiriro?
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2024
  • Nkhani Yofanana
  • Muzisonyeza Kuti Mumakhulupirira Malonjezo a Yehova
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2016
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2024
w24.06 103

MAWU A M’BAIBULO

Kodi Muli ndi Chikhulupiriro?

Kuti tizisangalatsa Yehova, tiyenera kukhala ndi chikhulupiriro. Komabe Baibulo limanena kuti “si anthu onse amene ali ndi chikhulupiriro.” (2 Ates. 3:2) Polankhula mawu amenewa, mtumwi Paulo ankanena za “anthu oipa kwambiri” omwe ankamuzunza ndipo ankafuna kupulumutsidwa kwa iwo. Koma zimene ananena pa nkhani ya chikhulupiriroyi zimakhudzanso anthu ena. Anthu ena safuna kuvomereza umboni woti kuli Mlengi. (Aroma 1:20) Anthu ena anganene kuti amakhulupirira Mulungu. Koma chikhulupiriro chimenechi si chomwe chimafunika kuti munthu azisangalatsa Yehova.

Tiyenera kukhulupirira kuti Yehova alipo ndiponso kuti amapereka mphoto kwa anthu amene ali ndi chikhulupiriro cholimba. (Aheb. 11:6) Chikhulupiriro ndi khalidwe limene munthu amakhala nalo mothandizidwa ndi mzimu woyera. Choncho kupemphera kwa Yehova, kungamuthandize munthu kuti alandire mzimuwu. (Luka 11:9, 10, 13) Njira inanso yaikulu imene munthu angalandirire mzimu woyera ndi kuwerenga Mawu a Mulungu omwe anawauzira pogwiritsa ntchito mzimuwo. Kenako, tiziganizira mozama zimene tawerenga n’kugwiritsa ntchito zomwe taphunzirazo. Tikamachita zimenezi, mzimu wa Yehova udzatithandiza pa moyo wathu ndipo tidzakhala ndi chikhulupiriro chomwe chimamusangalatsa.

    Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
    • tumizirani
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • zachinsinsi
    • JW.ORG
    • Lowani
    tumizirani