Mawu a M'munsi
a Polemba buku lake la Uthenga Wabwino, Luka anatchula Teofilo kuti ndi “wolemekezeka kwambiri.” (Luka 1:3) Anthu ena amaganiza kuti mwina Teofilo anali ndi udindo winawake, ndipo pa nthawiyo anali asanakhale wokhulupirira. Koma polemba buku la Machitidwe, Luka anangomutchula kuti “a Teofilo.” Akatswiri ena a Baibulo amaganiza kuti Teofilo anakhala wokhulupirira atawerenga Uthenga Wabwino wa Luka. Iwo amati n’chifukwa chake Luka sanam’tchulenso ndi mawu aulemu akuti “wolemekezeka kwambiri,” koma anamulembera monga m’bale wake wauzimu.