Mawu a M'munsi
a Katswiri wina ananena kuti pa nthawiyo panali lamulo la Kaisara limene linkaletsa munthu aliyense kulosera kuti “kudzabwera mfumu ina kapena ufumu, umene akuganiza kuti udzagonjetsa kapena kuweruza mfumu ya Roma imene inkalamulira pa nthawiyo.” Adani a Paulo ayenera kuti anapotoza uthenga wa mtumwiyu kuti aoneke ngati waphwanya lamulo limeneli. Onani bokosi lakuti “Olamulira a Roma M’nthawi ya Atumwi.”