Mawu a M'munsi
e Paulo anagwira mawu a ndakatulo ina (yotchedwa Phaenomena) ya zinthu zakuthambo yolembedwa ndi Aratus, wolemba ndakatulo wa m’gulu la Sitoiki. Mawu ofanana ndi amenewa amapezeka m’nkhani zina za Chigiriki, ndiponso mu nyimbo zotamanda Zeu zolembedwa ndi Cleanthes, wolemba mabuku wa m’gulu la Sitoiki.