Mawu a M'munsi
c Zikuoneka kuti Tito, yemwe anali Mkhristu wa Chigiriki amene anadzakhala mnzake wodalirika wa Paulo komanso mtumiki wake, anali m’gulu la anthu amenewa, omwe anatumizidwa ku Yerusalemu. (Agal. 2:1; Tito 1:4) Munthu ameneyu anali chitsanzo chabwino cha munthu wosadulidwa wa mtundu wina amene anadzozedwa ndi mzimu woyera.—Agal. 2:3.