Mawu a M'munsi
c Akatswiri ena amanena kuti amunawo anachita lumbiro lokhala Anaziri. (Num. 6:1-21) N’zoona kuti Chilamulo cha Mose chimene chinali ndi mfundo zokhudza lumbiro limenelo chinali chitasiya kugwira ntchito. Komabe, Paulo ayenera kuti anaganiza kuti palibe cholakwika chilichonse ngati amunawo atachita zimene analumbira kwa Yehova. Choncho panalibe cholakwika kuti awalipirire zonse zofunika ndiponso kupita nawo limodzi. Sitikudziwa lumbiro limene anthuwo anachita. Komabe, zikuoneka kuti Paulo sakanawathandiza kuti apereke nsembe ya nyama (ngati mmene Anaziri ankachitira), chifukwa ankadziwa kuti nsembeyo singathandize munthu kukhala oyera ku machimo ake. Nsembe yangwiro ya Khristu inachititsa kuti nsembe za nyama zisakhalenso ndi mphamvu yochotsa machimo. Sitikudziwa zonse zimene Paulo anachita, komabe tikukhulupirira kuti sakanavomera kuchita chilichonse chosemphana ndi chikumbumtima chake.