Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano

Mawu a M'munsi

c Nkhani imeneyi ikusonyeza zinthu ziwiri zopanda ulemu zimene ana a Eli ankachita. Chilamulo chinaneneratu zigawo za nyama yoperekedwa nsembe zimene ansembe ankayenera kudya. (Deut. 18:3) Koma ansembe oipawa anayamba kuchita zawozawo. Iwo ankauza anthu owathandizira kuti azipisa ndi chifoloko chachikulu m’miphika ya nyama ili pamoto n’kusankha nthuli iliyonse imene akufuna. Komanso anthu akabweretsa nsembe zawo kuchihema kuti azipereke paguwa la nsembe, ansembewo ankachititsa owathandizira awo kuchitira chipongwe anthu odzapereka nsembewo. Iwo ankakakamiza anthuwo kuti aziwapatsa nyama yosaphika, ngakhale asanapereke mafuta a nyamayo ngati nsembe kwa Yehova.—Lev. 3:3-5; 1 Sam. 2:13-17.

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani