Mawu a M'munsi
a Mawu oti “abale” angagwiritsidwenso ntchito ponena za alongo. Mwachitsanzo, Paulo ananena m’kalata yake yopita kwa Aroma kuti akulembera “abale.” Koma mawu amenewa ankatanthauzanso alongo chifukwa ena mwa alongowo anawatchula mayina awo. (Aroma 16:3, 6, 12) Ndipotu Nsanja ya Olonda yakhala ikugwiritsa ntchito mawu oti ‘abale ndi alongo’ pofotokoza za Akhristu.