Mawu a M'munsi
a Anthu ofufuza zinthu zakale anapeza zokolola zambiri zimene zinakwiririka pamalo amene panali mzinda wa Yeriko ndipo izi zikusonyeza kuti mzindawu sunazunguliridwe ndi Aisiraeli kwa nthawi yaitali moti chakudya sichinathe mumzindawo. Popeza Aisiraeli sanaloledwe kulanda zinthu mumzinda wa Yeriko, nthawi imene anagonjetsa mzindawu inali yabwino chifukwa m’minda munali chakudya chambirimbiri.—Yos. 5:10-12.