Mawu a M'munsi
a Lemba la chaka cha 2019, likutipatsa zifukwa zitatu zotithandiza kuti tisamade nkhawa ngakhale zinthu zoipa zitachitika m’dzikoli kapena pa moyo wathu. Nkhaniyi ifotokoza zifukwa zitatuzo ndipo itithandiza kuti tisamade nkhawa kwambiri koma tizidalira Yehova. Muziliganizira kwambiri lemba la chakali ndipo muliloweze ngati mungakwanitse. Lembali likuthandizani kwambiri pa mavuto amene mungakumane nawo m’tsogolo.