Mawu a M'munsi
a Nthawi zina, abale ndi alongo amene akuchita utumiki wa nthawi zonse amafunika kusiya utumiki kapena amapatsidwa utumiki watsopano. Munkhaniyi, tikambirana mavuto amene amakumana nawo komanso zimene angachite kuti asavutike kuzolowera. Tionanso zimene ena angachite powathandiza komanso mfundo zomwe zingathandize tonsefe zinthu zikasintha pa moyo wathu.