Mawu a M'munsi
a Tikukhala mu nthawi yapadera. Maulosi a m’buku la Chivumbulutso akukwaniritsidwa masiku ano. Kodi maulosiwo amatikhudza bwanji? Nkhaniyi komanso ziwiri zotsatira zifotokoza mfundo zina zomwe zili m’buku la Chivumbulutso. Zitithandizanso kudziwa mmene kutsatira mfundozo kungathandizire kuti kulambira kwathu kukhale kovomerezeka kwa Yehova Mulungu.