Mawu a M'munsi
c M’mbuyomu tinkafotokoza kuti mawu akuti ‘kuweruzidwa’ omwe atchulidwa palembali, amatanthauza kupatsidwa chilango kapena chigamulo pa zolakwa zimene munthu wachita. N’zoona kuti mawuwa angatanthauzenso zimenezo. Koma pa nkhaniyi, zikuoneka kuti Yesu anagwiritsa ntchito mawu akuti ‘kuweruzidwa’ ponena za kuyang’ana winawake mosamala n’cholinga chofuna kumuyesa, kapena monga mmene buku lotanthauzira Baibulo lina la Chigiriki linanenera kuti, “kuyang’anitsitsa khalidwe la winawake.”