Mawu a M'munsi
a Nkhaniyi ifotokoza zinthu zitatu zimene Yehova amachita pothandiza atumiki ake kuti azipirira mavuto mosangalala. Tiphunzira zinthu zimenezi pokambirana Yesaya chaputala 30. Kukambirana chaputalachi kutikumbutsa kufunika kopemphera kwa Yehova, kuphunzira Mawu ake komanso kuganizira mozama madalitso amene timapeza panopa ndiponso amene tidzapeze m’tsogolo.