Mawu a M'munsi
a Mtumwi Paulo analangiza Akhristu anzake kuti asamaganize kapena kuchita zinthu potengera nzeru za nthawi ino. Malangizo amenewatu ndi othandizanso kwa ife masiku ano. Sitiyenera kulola kuti zochitika za m’dzikoli zizikhudza kaganizidwe ndi zochita zathu ngakhale pang’ono. Kuti izi zitheke, tiyenera kupitiriza kusintha kaganizidwe kathu ngati tazindikira kuti sikakugwirizana ndi zimene Mulungu amafuna. Munkhaniyi, tikambirana mmene tingachitire zimenezi.