Mawu a M'munsi
a Tikamakumana ndi mayesero ovuta tisamaganize kuti Yehova sakutithandiza. Nthawi zina tingamaone ngati zinthu zatiyendera bwino mayeserowo akatha. Komabe zimene zinachitikira Yosefe zikutiphunzitsa mfundo yofunika kwambiri yakuti Yehova angatithandize kuti zinthu zizitiyenderabe bwino ngakhale pa nthawi imene tikukumana ndi mayesero. Munkhaniyi tiona mmene iye amachitira zimenezi.