Mawu a M'munsi
a Pa nyengo ya Chikumbutso timalimbikitsidwa kuti tiziganizira moyo wa Yesu ndi imfa yake komanso chikondi chimene iye ndi Atate wake anatisonyeza. Kuchita zimenezi kungatithandize kuti tiziwayamikira. Nkhaniyi isonyeza njira zimene tingasonyezere kuti timayamikira dipo komanso kuti timakonda Yehova ndi Yesu. Tionanso mmene zimenezi zingatilimbikitsire kuti tizikonda abale ndi alongo athu, tizikhala olimba mtima ndiponso tizisangalala ndi utumiki wathu.