Mawu a M'munsi
c Mariya ankadziwa bwino Malemba ndipo ankawafotokoza. (Luka 1:46-55) N’zoonekeratu kuti Yosefe ndi Mariya sakanakwanitsa kukhala ndi buku lawolawo la Malemba. Ayenera kuti ankamvetsera mwatcheru Mawu a Mulungu akamawerengedwa ku sunagoge n’cholinga choti aziwakumbukira pambuyo pake.