Mawu a M'munsi
a Ubatizo ndi wofunika kwambiri kwa wophunzira Baibulo aliyense. Kodi n’chiyani chingathandize wophunzira Baibulo kuti abatizidwe? Mawu amodzi, chikondi. Kukonda chiyani komanso ndani? Munkhaniyi tipeza mayankho a mafunso amenewa komanso tikambirana mmene moyo wa Mkhristu wobatizidwa umayenera kukhalira.