Mawu a M'munsi
a Chilengedwe cha Yehova n’chodabwitsa. Timachita chidwi ndi zinthu zimene anapanga monga mphamvu yodabwitsa ya dzuwa komanso tinthu tosalimba ngati maluwa. Chilengedwe chingatithandizenso kuzindikira makhalidwe a Yehova. Munkhaniyi, tikambirana chifukwa chake tiyenera kumapeza nthawi yophunzira zinthu zam’chilengedwe komanso mmene kuchita zimenezi kungatithandizire kukhala pa ubwenzi wolimba ndi Mulungu wathu.