Mawu a M'munsi
a Abale ndi alongo ambiri amakumbukirabe nthawi imene anasangalala kuona zinthu zachilengedwe limodzi ndi makolo awo. Amakumbukiranso mmene makolo awo anagwiritsira ntchito nthawi imeneyo powaphunzitsa zokhudza makhalidwe a Yehova. Ngati muli ndi ana, kodi mungagwiritse ntchito bwanji chilengedwe powaphunzitsa zokhudza makhalidwe a Mulungu? Nkhaniyi iyankha funso limeneli.