Mawu a M'munsi
a Anthu ambiri masiku ano sakhulupirira lonjezo la m’Baibulo lokhudza dziko latsopano. Iwo amaona kuti zimenezi ndi maloto chabe, kapena kuti zinthu zomwe sizingachitike. Komabe ifeyo sitikayikira kuti malonjezo onse a Yehova adzakwaniritsidwa. Ngakhale zili choncho, tiyenera kupitiriza kulimbitsa chikhulupiriro chathu. Motani? Nkhaniyi ifotokoza mmene tingachitire zimenezi.