Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • sjj 96
  • Baibulo Ndi Chuma

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Baibulo Ndi Chuma
  • Imbirani Yehova Mosangalala
  • Nkhani Yofanana
  • Bwerani kwa Mulungu Kuti Mupulumuke
    Imbirani Yehova Mosangalala
  • Mudalitse Msonkhano Wathu
    Imbirani Yehova Mosangalala
  • Tizikonda ndi Mtima Wonse Chuma Chimene Mulungu Watipatsa
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2017
  • Yehova Wayamba Kulamulira
    Imbirani Yehova Mosangalala
Onani Zambiri
Imbirani Yehova Mosangalala
sjj 96

NYIMBO 96

Baibulo Ndi Chuma

zosindikizidwa

(Miyambo 2:1)

  1. 1. Pali buku limene mawu ake

    Amatibweretsera chimwemwe.

    Mfundo zake zodabwitsa n’zamphamvu,

    Limapatsa nzeru owerenga.

    Bukuli ndi Baibulo loyera.

    Olilemba anauziridwa.

    Ankakonda Yehova M’lungu wawo,

    Mzimu wake unawathandiza.

  2. 2. Analemba zokhudza chilengedwe,

    Mmene M’lungu anachilengera.

    Analembanso za Paradaiso

    Ndiponso za mmene anathera.

    Analemba za mngelo winawake

    Amene ananyoza Yehova.

    Anabweretsa mavuto pa anthu

    Koma Yehova adzapambana.

  3. 3. Masiku ano tikusangalala

    Ufumu wa Mulungu wayamba.

    Tiuze anthu uthenga wabwino

    Ndi madalitso omwe abwere.

    M’Baibulo muli zosangalatsa.

    Chakudya chochuluka kwambiri.

    Limatipatsa mtendere wambiri,

    Tiyesetse kumaliwerenga.

(Onaninso 2 Tim. 3:​16; 2 Pet. 1:​21.)

    Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
    • tumizirani
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • zachinsinsi
    • JW.ORG
    • Lowani
    tumizirani