7 Anthu a kumeneko anali kufunsa za mkazi wake, ndipo iye anali kuwayankha kuti, “Ndi mlongo wanga.”+ Anali kuopa kunena kuti: “Ndi mkazi wanga,” chifukwa malinga ndi kunena kwake, anati: “Anthu a kuno andipha chifukwa cha Rabeka,” pakuti mkaziyo anali wokongola mochititsa kaso.+