11 “‘Kumayambiriro kwa mwezi uliwonse, muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Nsembeyo izikhala ng’ombe ziwiri zazing’ono zamphongo, nkhosa imodzi yamphongo, ndi ana a nkhosa 7 amphongo opanda chilema. Mwana wa nkhosa aliyense azikhala wachaka chimodzi.+