17 Simudzaloledwa kudyera m’mizinda yanu chakhumi cha mbewu zanu,+ vinyo wanu watsopano, mafuta anu, ana oyamba kubadwa a ng’ombe zanu ndi a nkhosa zanu,+ iliyonse mwa nsembe zanu za lonjezo zimene mudzalonjeza, nsembe zanu zaufulu+ kapena chopereka chochokera m’manja mwanu.+