-
Nehemiya 8:10Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
10 Nehemiya anapitiriza kunena kuti: “Pitani mukadye zinthu zonona, kumwa zinthu zokoma ndi kugawa chakudya+ kwa anthu amene sanathe kudzikonzera chakudya, pakuti lero ndi tsiku lopatulika kwa Ambuye wathu. Choncho musadzimvere chisoni pakuti chimwemwe chimene Yehova amapereka ndicho malo anu achitetezo.”
-
-
Esitere 9:22Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
22 Anawalamula kuti masiku amenewa akhale ochita phwando, kusangalala, kutumizirana chakudya+ ndi kupereka mphatso kwa anthu osauka.+ Anatero pakuti amenewa ndi masiku amene Ayuda anasiya kuvutitsidwa ndi adani awo,+ komanso mwezi umene chisoni chawo chinasintha kukhala chikondwerero ndiponso pamene tsiku lolira+ linasintha kukhala tsiku losangalala.
-