19 Ine ndanena kuti, ‘Mokondwera ndinakuikani pakati pa ana anga ndi kukupatsani dziko labwino,+ cholowa chimene mitundu yambiri ya anthu imachisirira!’ Ndipo ndinanenanso kuti, ‘Anthu inu mudzandiitana kuti, “Atate wanga!”+ ndipo mudzandilondola osabwerera.’