21 Iwe Oholiba, unapitiriza kulakalaka khalidwe lotayirira la pa utsikana wako mwa kufunafuna njira zoti amuna atsamire pachifuwa chako, kuyambira pamene unali ku Iguputo+ mpaka m’tsogolo. Unachita izi kuti ukhutiritse chilakolako cha mabere a utsikana wako.+