5 “Tsopano kodi pamenepa ndichitepo chiyani?” akutero Yehova. “Pakuti anthu anga anatengedwa popanda malipiro alionse.+ Amene anali kuwalamulira ankangokhalira kufuula.+ Nthawi zonse, tsiku lonse lathunthu, dzina langa anali kulichitira chipongwe,”+ akutero Yehova.