11 Kenako mzimu+ unandinyamula+ n’kupita nane kuchipata cha kum’mawa cha nyumba ya Yehova chimene chinayang’ana mbali ya kum’mawa.+ Pakhomo la chipatacho ndinaonapo amuna okwanira 25.+ Pakati pawo ndinaonapo Yaazaniya mwana wa Azuri ndi Pelatiya mwana wa Benaya. Amuna onsewo anali akalonga.+