33 “Pangano+ limene ndidzapangane ndi nyumba ya Isiraeli pambuyo pa masiku amenewo ndi ili:+ Ndidzaika chilamulo changa mwa iwo+ ndipo ndidzachilemba mumtima mwawo.+ Ine ndidzakhala Mulungu wawo ndipo iwo adzakhala anthu anga,”+ watero Yehova.
21 akukonzekeretseni ndi chilichonse chabwino kuti muchite chifuniro chake. Ndipo kudzera mwa Yesu Khristu, achite mwa ife zimene zili zokondweretsa pamaso pake.+ Kwa iye kukhale ulemerero kwamuyaya.+ Ame.