Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Levitiko 24:5, 6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Utenge ufa wosalala nʼkuphika mikate 12 yozungulira yoboola pakati. Mkate uliwonse uzipangidwa ndi ufa wokwanira magawo awiri mwa magawo 10 a muyezo wa efa.* 6 Ndipo usanjikize mikateyo mʼmagulu awiri. Gulu lililonse likhale ndi mikate 6.+ Uike mikateyo patebulo lagolide woyenga bwino pamaso pa Yehova.+

  • 1 Samueli 21:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Choncho wansembeyo anamupatsa mkate wopatulika,+ chifukwa panalibe mkate wina koma mkate wachionetsero umene anauchotsa pamaso pa Yehova tsiku limenelo kuti aikepo watsopano.

  • 1 Mbiri 9:32
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 32 Abale awo ena, mbadwa za Kohati, ankayangʼanira mikate yosanjikiza,*+ kuti aziikonza pa tsiku lililonse la Sabata.+

  • 2 Mbiri 13:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Iwo akupereka nsembe zopsereza kwa Yehova mʼmawa uliwonse+ ndi madzulo alionse limodzi ndi mafuta onunkhira.+ Ndipo mikate yosanjikiza*+ ili patebulo la golide woyenga bwino. Komanso madzulo alionse+ amayatsa nyale zomwe zili pachoikapo nyale chagolide.+ Tikuchita zimenezi chifukwa tikukwaniritsa udindo wathu kwa Yehova Mulungu wathu, koma inuyo mwamusiya.

  • Mateyu 12:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Iye analowa mʼnyumba ya Mulungu ndipo anadya mitanda ya mkate woonetsa kwa Mulungu,*+ umene iye ndi anthu omwe anali nawo aja sankayenera kudya malinga ndi malamulo, koma ansembe okha.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena